Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Amunjata kaamba koba zipangizo za ESCOM

Apolisi m’boma la Balaka anjata a Paul Lipenga, 46, powaganizira kuti anaononga komanso kuba nthambo za magetsi za ESCOM.

Ofalitsa nkhani pa polisi ya m’boma la Balaka, a Gladson M’bumpha, wati a Lipenga anapalamula mlanduwo pa 22 November chaka chino pa sitolo za pa Mbera m’bomalo.

A M’bumpha anati anthu ena akufuna kwabwino ndiwo anatsina khutu apolisiwo zokhuza nkhaniyi.

Apolisi atachita kafukufuku anapeza Lipenga ali ndi nthambo za ESCOM zotalika mamita 300 za ndalama zoposa K5 million.

Pakadali pano, apolisiwa ati ndi okhutira ndi momwe akugwilira ntchito pamodzi ndi anthu m’bomalo maka pofuna kuthetsa umbanda ndi umbava.

Olemba: Alufeyo Liyaya

Related posts

Zaka zitatu pogulitsa makala mosatsata lamulo

Mayeso Chikhadzula

Parliament amends bill to revise investment into Salima – Lilongwe Water project

Romeo Umali

Irish Ambassador donates K5.3 million for Paris 2024 Paralympics

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.