Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Amunjata kaamba koba zipangizo za ESCOM

Apolisi m’boma la Balaka anjata a Paul Lipenga, 46, powaganizira kuti anaononga komanso kuba nthambo za magetsi za ESCOM.

Ofalitsa nkhani pa polisi ya m’boma la Balaka, a Gladson M’bumpha, wati a Lipenga anapalamula mlanduwo pa 22 November chaka chino pa sitolo za pa Mbera m’bomalo.

A M’bumpha anati anthu ena akufuna kwabwino ndiwo anatsina khutu apolisiwo zokhuza nkhaniyi.

Apolisi atachita kafukufuku anapeza Lipenga ali ndi nthambo za ESCOM zotalika mamita 300 za ndalama zoposa K5 million.

Pakadali pano, apolisiwa ati ndi okhutira ndi momwe akugwilira ntchito pamodzi ndi anthu m’bomalo maka pofuna kuthetsa umbanda ndi umbava.

Olemba: Alufeyo Liyaya

Related posts

Chakwera congratulates Malawian on becoming mayor of Farnham in the UK

Rabson Kondowe

S.I.N.A drops debut single

Romeo Umali

Chakwera arrives at MSG Kanengo Campus

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.