Malawi Broadcasting Corporation
Local News

Airtel Malawi yataya ndalama (loss) zokwana K15 billion chaka chatha

Kampani ya Airtel Malawi siyinapange phindu lililonse chaka chatha ndipo m’malo mwake, yataya ndalama (loss) za pakati pa K15.1 billion mpaka K15.7 billion.

Izi ndimalinga ndi kalata yochokera ku Airtel yonena m’mene akuwonera kuti chuma cha kampaniyi chayenda bwanji chaka chatha.

Kalatayi ikudza Airtel Malawi itawerengeranso za chuma chake cha chaka chatha.

Kalata yoyamba inaawonetsa kuti kusapanga phinduku kunali pa K2 billion koma kalata yatsopanoyi ikuti kwakwera atawonkhotsera ndalama zina zama dollar zokhudzana ndikubwereka zipangizo zothandizira ntchito yawo.

Airtel Malawi ndi imodzi mwa kampani za lamya m’dziko muno zomwe ziri pa msika wamasheya wa Malawi Stock Exchange.

Related posts

Abwenzi a Boma pachitukuko alonjeza thandizo pantchito zachuma

Rabson Kondowe

Vandalism hinders MAREP 9 progress — Govt

Romeo Umali

Osagwiritsa ntchito imfa ya Chilima pa ndale

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.