Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Adzudzula zipani zomwe zikufuna kuti MEC isagwiritse chiphaso cha unzika pazisankho

Gulu lina la a Malawi omwe akudzitchula kuti  Mzika Zokhudzidwa ladzudzula mchitidwe wa zipani zina zandale zimene zikufuna kukakamiza bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) kuti lisinthe ndondomeko yogwiritsa ntchito chiphaso cha unzika pa chisankho cha chaka chamawa.

Malinga ndi wapampando wa gululi, a Agape Khombe, malamulo a dziko lino akufotokoza momveka bwino kuti kulembetsa mkaundula wa mavoti pakufunika chiphaso chaunzika ndipo anatsindika kuti mmalawi aliyense okonda dziko lake sangatsutsane ndi mfundoyi.

A Khombe ati monga mzika zokhudzidwa, gulu lawo likudabwa kuti ena omwe akutsutsa za nkhaniyi ndi aphungu amene anakhazikitsa nawo lamuloli kunyumba yamalamulo.

Pamenepa, akuluakulu agululi, omwe anatsogozedwa ndi a Billy Malata, akuti a Malawi azindikire kuti chisankho ndi chinthu chofunika kuchiteteza poonetsetsa kuti mzika zokha zadziko lino ndizo zikuponyadi voti.

Related posts

President Chakwera wakhazikiska Committee ya nduna kwendeska nyifwa ya Chilima

MBC Online

Young Scorchers eye first World Cup appearance

Romeo Umali

Perekani mauthenga achisankho mosakondera – MEC

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.