Malawi Broadcasting Corporation
Africa Local News Nkhani Politics

“MALONDA AFUNIKA PA CHIPATA CHA MWANZA” – CHAKWERA

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr. Lazarus Chakwera, wati chipata cha Mwanza ndi chofunika kuti kuzikhala malonda zomwe zingathe kubweretsa chitukuko m’Bomali.

Chipata-chi ndi chatsopano ndipo amene azatsegule ndi Dr. Chakwera pamodzi mtsogoleri wa dziko la Mozambique a Felipe Nyusi.

Boma, kudzera ku bungwe lotolera misonkho la Malawi Revenue authority (MRA), linamanga malowa ngati njira imodzi yowonetsetsa kuti anthu sakumatenga nthawi yayitali pofuna kulowa kapena kutuluka m’dziko lino.

Mtsogoleri wa dziko la Malawi, Dr. Lazarus Chakwera.Posachedwapa, anthu ochita ntchito malonda, monga oyendetsa galimoto zonyamula katundu, akhala akudandaula zakuchedwa kwa ndondomeko zoti alowe kapena atuluke m’dziko lino.

Malo a mtundu otere-wu akugwira kale ntchito m’maboma a Mchinji komanso Dedza.

Olemba : Timothy Kateta

Related posts

Police officer donates school uniform in Lilongwe

Romeo Umali

Cultural festivals are crucial for tourism — Mzuzu City Council

Romeo Umali

MACRA renews MTL’s licenses

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.