Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

ACHINYAMATA A CHIPANI CHA MCP ATHANDIZA PACHIPATALA CHA AREA 25 KU LILONGWE

Gulu la achinyamata a chipani cha Malawi Congress lotchedwa MCP Youth League lapereka katundu osiyana siyana kwa odwala mu chipinda chochilira amai pachipatala chaching’ono cha Area 25 ku Lilongwe.
Achinyamatawa anakonzanso pa chipatalachi.

Wapampando wagululi, a Emmanuel Thembachako, wati apereka katundu komanso kukonza pachipatalachi ngati mbali imodzi yantchito zachifundo zomwe achinyamatawa amagwira.

“Taperekanso katunduyu ndikukonzaso pachipatala pano pofuna kuonetsera utsogoleri wachipani chathu kuti umaika chisamaliro cha anthu patsogolo,” anatero a Thembachako.

MCP Youth League kusesa pa chipatala cha Area 25

Namwino oyang’anira chipinda chochilira amai pa chipatalachi, a Amina Banda, anati katunduyu athandiza odwala ambiri omwe amasowa zakudya pa nthawi yomwe ali pachipatalapa.

A Banda ayamikiranso achinyamatawa potchetcha malo ozungulira chipatalachi ndikusesa ponena kuti zithandiza odwala ndi ogwira ntchito kukhala malo aukhondo.

Wina mwa katundu yemwe apereka kwa odwala omwe anawapeza mu chipinda chochilira amai ndi monga sopo, sugar ufa komanso ndiwo za soya.

Related posts

MBC yasintha matchanelo pa DSTV, GOTV

Rabson Kondowe

Greenbelt yagulitsa matumba opyola 3,000 ku NFRA

Romeo Umali

President Chakwera akayendera ntchito zachitukuko kumpoto

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.