Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

A Nankhumwa akhazikitsa chipani

Mtsogoleri wa chipani chatsopano cha People’s Development (PDP), Kondwani Nankhumwa, wati chipanichi chabwera kudzasintha Malawi kukhala dziko lodzidalira pa chakudya, la umodzi ndinso kulimbikira pantchito.

Poyankhula pamsonkhano wa atolankhani mumzinda wa Blantyre, iwo ati chipanichi chithetsa m’chitidwe okakamira m’maudindo muzipani.

A Nankhumwa atinso a Malawi akufunika chipani chomwe chingamalore anthu kupikisana momasuka.

Wolemba: Blessings Cheleuka

Related posts

Boma layamikira ntchito za NASCENT Solutions polimbikitsa maphunziro

Alinafe Mlamba

‘Alimi akonzeke kunyotsolerana K14M’

Rabson Kondowe

Phungu wa DPP wayamikira boma chifukwa chosakondera

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.