Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

A Nankhumwa akhazikitsa chipani

Mtsogoleri wa chipani chatsopano cha People’s Development (PDP), Kondwani Nankhumwa, wati chipanichi chabwera kudzasintha Malawi kukhala dziko lodzidalira pa chakudya, la umodzi ndinso kulimbikira pantchito.

Poyankhula pamsonkhano wa atolankhani mumzinda wa Blantyre, iwo ati chipanichi chithetsa m’chitidwe okakamira m’maudindo muzipani.

A Nankhumwa atinso a Malawi akufunika chipani chomwe chingamalore anthu kupikisana momasuka.

Wolemba: Blessings Cheleuka

Related posts

Anthu ochuluka asonkhana ku maliro a Hope Chisanu

Romeo Umali

Abusa asiye kudalira nkhosa zawo pachuma

Rabson Kondowe

Ngongole ya maphunziro ndi yofunika kwambiri — Kabwila

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.