Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Apolisi amanga mlonda pomuganizira kuti anaba

Apolisi m’boma la Mangochi amanga a Smith White, 32, powaganizira kuti anaba zipangizo zomangira nyumba za K30 million ku Savijan Cottage komwe amagwirako ntchito ngati mlonda.

Ofalitsa nkhani ku Polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daud, ati atachita kafukufuku anapeza kuti a White anagulitsa katunduyi yemwe amangokhala.

A Daudi ati mwini wakeyo atazindikira izi, anakanena ku polisi ndipo apolisiwo anapeza wina mwa katunduyi yemwe ndi wa ndalama zokwana K20 million.

 

Related posts

Live event happening now at COMESA

Alick Sambo

Number of children accessing HIV & AIDS services spikes in CZ

Romeo Umali

Government commits to youth development through digital initiatives

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.