Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Apolisi amanga mlonda pomuganizira kuti anaba

Apolisi m’boma la Mangochi amanga a Smith White, 32, powaganizira kuti anaba zipangizo zomangira nyumba za K30 million ku Savijan Cottage komwe amagwirako ntchito ngati mlonda.

Ofalitsa nkhani ku Polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daud, ati atachita kafukufuku anapeza kuti a White anagulitsa katunduyi yemwe amangokhala.

A Daudi ati mwini wakeyo atazindikira izi, anakanena ku polisi ndipo apolisiwo anapeza wina mwa katunduyi yemwe ndi wa ndalama zokwana K20 million.

 

Related posts

Mwambo wa maliro a Hope Chisanu wayamba

Romeo Umali

Malawi to benefit from IEA summit on clean cooking in Africa

Blessings Kanache

Government installs new cargo X-ray machine at KIA

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.