Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Apolisi amanga mlonda pomuganizira kuti anaba

Apolisi m’boma la Mangochi amanga a Smith White, 32, powaganizira kuti anaba zipangizo zomangira nyumba za K30 million ku Savijan Cottage komwe amagwirako ntchito ngati mlonda.

Ofalitsa nkhani ku Polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daud, ati atachita kafukufuku anapeza kuti a White anagulitsa katunduyi yemwe amangokhala.

A Daudi ati mwini wakeyo atazindikira izi, anakanena ku polisi ndipo apolisiwo anapeza wina mwa katunduyi yemwe ndi wa ndalama zokwana K20 million.

 

Related posts

IT firm touts AI-driven financial inclusion

Romeo Umali

Clement Nyondo: From league struggles to Castel Challenge Cup hero

Romeo Umali

Sitilora kuti atichitse manyazi pakhomo — Mpinganjira

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.