Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Burning Spear atsanzikana ndi anthu asanapume kuimba

Omwe akuyendetsa phwando la nyimbo la Burning Spear atsimikiza kuti phwandoli litheka kaamba koti ichi ndi chikonzero chake kuti adzayimbe ku Malawi asanapume kuimba.

Mkulu wa Sound Addicts, a Shadreck Kalukusha pamodzi ndi a Sound System Club & Bon Afrikan Productions, ati zonse zili mchimake ndipo katswiri wa chamba cha Reggae yu abwera ndi gulu lake la anthu 17.

Burning Spear yemwe ali ndi zaka 79 ndipo akuyembekezeka kupuma pamaimbidwe, adzaimba m’dziko muno pabwalo Civo mwezi wa October.

Malawi ndi limodzi mwa maiko asanu ndi limodzi omwe nsalamangweyi iyimbe isanpume.

Izi zikutanthauza kuti aka kakhala koyamba ndikotsiriza  kuimba kuno ku Malawi.

 

Olemba: Emmanuel Chikonso

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Veteran broadcaster Madise to be laid to rest in Mzimba

MBC Online

Ayamikira Dr Chakwera posankha mabodi atsopano a kampani zaboma

MBC Online

Chakwera calls for collective effort in the business sector

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.