Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ayamikira Dr Chakwera posankha mabodi atsopano a kampani zaboma

Ena mwa atsogoleri amipingo m’dziko muno ati mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera waonetsa kusakondera kwake posankha anthu atsopano m’ma board a kampani za boma.

Prezidenti Chakwera posachedwapa wasankha anthu atsopano kuti athe kutumikira m’ma board a kampanizi.

Chikalata chomwe bungwe lalikulu lama Sheikh m’dziko muno la Ulama Council latulutsa chati Dr Chakwera waonetseratu poyera kuti boma lake limaganizira kwambiri kuti anthu achipembezo cha chisilamu atha kuthandiza nawo kupititsa  patsogolo chitukuko cha dziko lino.

M’mau ake, mlembi wamkulu wa mpingo wa Livingstonia CCAP Synod, m’busa William Tembo, anati zomwe Prezidenti Chakwera wachita zithandiza kulimbikitsa mgwirizano pakati anthu azipembedzo zosiyanasiyana m’dziko muno.

Pothilirapo ndemanga, m’busa Yolamu Nyirenda wati kampani komanso mabungwe osiyanasiyana m’dziko muno atengerepo phunziro posankha anthu mosaganizira zipembedzo komanso komwe akuchokera.

Mlangizi wa mtsogoleri wa dziko lino pa nkhani zachipembedzo, m’busa  Brian Kamwendo, wati Prezidenti Chakwera apitiriza kukwaniritsa mfundo zake zonse zomwe anawalonjeza aMalawi.

 

Olemba: George Banda

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Walipira chindapusa chifukwa chonyoza wodwala AIDS

Charles Pensulo

President Chakwera returns to Lilongwe

Kumbukani Phiri

Ochita bizinesi zing’onozing’ono apindula mu mgwirizano wa NBM ndi kampani zina

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.