Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Local Local News Nkhani

‘Mtayakhasu ndi ulimi othana ndi njala’

Alimi achitsanzo amene ali mu ndondomeko yokhala ndi chakudya chokwanira pakhomo alangiza alimi anzawo m’dziko muno kuti ayike chidwi paulimi wa mtayakhasu.

Iwowa ali mu nthambi yachitukuko ya mpingo wa Salvation Army imene ikugwira ntchito kwa mfumu yayikulu Mwanza m’ boma la Salima.

M’modzi wa alimi a chitsanzowa, a m’mudzi wa Chikhawo kuderali, a Matsaka Machira, ati ulimiwu ndi othandiza chifukwa amatha kukolola chimanga chambiri pamalo ochepa.

Iwo ati pa ulimi wachaka chino, akolola matumba 11 olemera ma kilogramme 50 limodzi pa munda wa mamita 39 mu litali ndi mamita 16.2 mulifupi, zomwe ati zithandize kuthana ndi vuto la njala chaka chino.

Mlangizi wa ndondomeko yolimbitsa ntchito zaunkhondo, kukhala ndi chakudya chokwanira pabanja komanso kupilira ku mpingowu, a Blessings Mwalwanda, anati ndi cholinga chawo kubweretsa njira zamakono za ulimi pothana ndi njala kaamba ka kusintha kwanyengo.

Pakadali pano, a Lloyd Tiopanyasi a m’mudzi wa Kachigulu, mfumu yayikulu Khombedza m’boma la Salima, apempha mpingowu kuti ufikirenso m’mudzi mwawo chifukwa ati njirayi ndi gwero la phindu paulimi m’dziko muno.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Tisewera kuti tibwezeretse ulemu wathu – Mabedi

Paul Mlowoka

Mafumu ku Mzimba apepesa Dr Chakwera

Beatrice Mwape

TOURISM PUBLIC BEACH PROJECT LAUNCHED IN SALIMA

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.