Malawi Broadcasting Corporation
Education Local Local News Nkhani Religion

Islamic Information yalimbikitsa achinyamata kuwerenga

Bungwe la Islamic Information Bureau munzinda wa Mzuzu lalimbikitsa achinyamata kuti akhale ndi mtima okonda kuwerenga mabuku ndi cholinga chakuti ziwathandize kuchita bwino pa maphunziro awo.

Mkulu wa bungweli, Sheikh Francis Iron, ayankhula izi pamapeto pa mpikisano owerenga bukhu m’mwezi wa Ramadhan lotchedwa ‘Chikhulupiliro cha Msilamu’ ndipo pamapeto pake opikisanawo anawafunsa mafunso.

“Izi zithandiza kuti akhale olimbika kuwerenga kuti adziwe za chipembezo chawo komanso ziwawonjezera chidwi choti adzikalimbikira kuwerenga ku Sukulu,” anatero a Iron.

Amene wapambana walandira K80,000 komanso bukhu la Quran, pamene opambana enawo alandira K50,000 ndi K30,000.

Olemba: Hassan Phiri

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MEC yalengeza zotsatira za chisankho cha komiti yayikulu ya DPP

Arthur Chokhotho

Renewable energy courses boosting energy sector — MZUNI

MBC Online

FISCAL POLICE NAB MULLI, MUHARA

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.