Malawi Broadcasting Corporation
Education Local Local News Nkhani Religion

Islamic Information yalimbikitsa achinyamata kuwerenga

Bungwe la Islamic Information Bureau munzinda wa Mzuzu lalimbikitsa achinyamata kuti akhale ndi mtima okonda kuwerenga mabuku ndi cholinga chakuti ziwathandize kuchita bwino pa maphunziro awo.

Mkulu wa bungweli, Sheikh Francis Iron, ayankhula izi pamapeto pa mpikisano owerenga bukhu m’mwezi wa Ramadhan lotchedwa ‘Chikhulupiliro cha Msilamu’ ndipo pamapeto pake opikisanawo anawafunsa mafunso.

“Izi zithandiza kuti akhale olimbika kuwerenga kuti adziwe za chipembezo chawo komanso ziwawonjezera chidwi choti adzikalimbikira kuwerenga ku Sukulu,” anatero a Iron.

Amene wapambana walandira K80,000 komanso bukhu la Quran, pamene opambana enawo alandira K50,000 ndi K30,000.

Olemba: Hassan Phiri

Related posts

Social Cash Transfer Programme to register 361,642 new beneficiaries

Rabson Kondowe

Maranatha Academy awards Malawi’s top MSCE students

McDonald Chiwayula

NBM sponsors MDF military drill

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.