Malawi Broadcasting Corporation
Crime Development Local Local News Nkhani

Zamanyazi: Mphunzitsi ogwililira akagwira ukaiyidi kwa zaka 20

Bwalo la milandu m’boma la Mangochi lalamula a Nelson Lipenga kuti akagwire ukaidi wa kalavula gaga kwa zaka makumi awiri (20) kaamba kopezeka olakwa pa mlandu ogwililira mwana wa zaka khumi ndi zisanu.

A Lipenga, amene ndi mphunzitsi, anzawo adawapezelera akuchita zadama ndi mwanayu pa nthawi imene anzake amawerenga.

M’bwalo la milandu, mtsikanayu adaulula kuti aphunzitsiwa akhala akugona naye mokakamiza kuyambira ali Standard 7 ndipo pano ali Standard 8 ndipo amaphunzira pa sukulu ya pulaimale ya Mama Khadidja, yomwe ndi ya atsikana okhaokha.

Ogamula mlandu, a Muhamad Chande, anati ndikutheka kuti a Lipenga adachita zimenezi ngati njira yobwezera chipongwe popeza mwana wawo adachitidwapo chipongwe choterechi.

Popereka chilango, a Chande adati limeneli likhale chenjezo kwa a bambo osaugwira mtima.

 

Related posts

World Vision applauds Senior Chief Kayembe’s efforts against early marriages

Alinafe Mlamba

Macra’s muuni fund empowers innovators

Romeo Umali

Kyungu urges transparency and accountability among duty bearers

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.