Malawi Broadcasting Corporation
Crime Development Local Local News Nkhani

Zamanyazi: Mphunzitsi ogwililira akagwira ukaiyidi kwa zaka 20

Bwalo la milandu m’boma la Mangochi lalamula a Nelson Lipenga kuti akagwire ukaidi wa kalavula gaga kwa zaka makumi awiri (20) kaamba kopezeka olakwa pa mlandu ogwililira mwana wa zaka khumi ndi zisanu.

A Lipenga, amene ndi mphunzitsi, anzawo adawapezelera akuchita zadama ndi mwanayu pa nthawi imene anzake amawerenga.

M’bwalo la milandu, mtsikanayu adaulula kuti aphunzitsiwa akhala akugona naye mokakamiza kuyambira ali Standard 7 ndipo pano ali Standard 8 ndipo amaphunzira pa sukulu ya pulaimale ya Mama Khadidja, yomwe ndi ya atsikana okhaokha.

Ogamula mlandu, a Muhamad Chande, anati ndikutheka kuti a Lipenga adachita zimenezi ngati njira yobwezera chipongwe popeza mwana wawo adachitidwapo chipongwe choterechi.

Popereka chilango, a Chande adati limeneli likhale chenjezo kwa a bambo osaugwira mtima.

 

Related posts

Tiyeni tigwirizane pokonda dziko – Chaponda

Mayeso Chikhadzula

Chinese EV manufacturer targets Zimbabwe, Malawi in Africa expansion drive

MBC Online

Flames open against Zambia in Four Nations Tournament

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.