Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

Zipani zikusowekera demokalase ndi umodzi, CCAP ya Livingstonia Sinodi yatero

Sinodi ya Livingstonia mu mpingo wa CCAP, pansi pa nthambi yake ya chilungamo ndi mtendere, yati mu zipani zambiri m’dziko muno mulibemo demokalase ndi umodzi.

A Mcbowman Mulagha, mkulu wa nthambiyi, wapeleka chitsanzo chammene zinthu ziliri m’chipani cha Democratic Progressive (DPP) ndi zipani zina.

Posachedwapa, chipani cha DPP chinachotsa ena mwa atsogoleri ake kaamba kophwanya ena mwa malamulo achipanichi.

A Mulagha ati zimenezi zili ndi kuthekera koononga ndale komanso kusokoneza anthu.

“Zipani zandale m’dziko muno ziyambe kutsatira mfundo za demokalase zomwe dziko lino linayamba kutsatira zaka zambiri zapitazo, choncho tipemphe atsogoleri azipanizi kuti alore mamembala ake kupikisana m’maudindo osiyanasiyana ndikupanga zokomera amalawi,” iwo anatero.

Olemba: George Mkandawire

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Chilima arrives in Korea

Timothy Kateta

Amai atatu ali mchitokosi pamulandu wakuba ku Mangochi

Davie Umar

Child injured as bus shelter collapses in Mangochi

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.