Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

Zipani zikusowekera demokalase ndi umodzi, CCAP ya Livingstonia Sinodi yatero

Sinodi ya Livingstonia mu mpingo wa CCAP, pansi pa nthambi yake ya chilungamo ndi mtendere, yati mu zipani zambiri m’dziko muno mulibemo demokalase ndi umodzi.

A Mcbowman Mulagha, mkulu wa nthambiyi, wapeleka chitsanzo chammene zinthu ziliri m’chipani cha Democratic Progressive (DPP) ndi zipani zina.

Posachedwapa, chipani cha DPP chinachotsa ena mwa atsogoleri ake kaamba kophwanya ena mwa malamulo achipanichi.

A Mulagha ati zimenezi zili ndi kuthekera koononga ndale komanso kusokoneza anthu.

“Zipani zandale m’dziko muno ziyambe kutsatira mfundo za demokalase zomwe dziko lino linayamba kutsatira zaka zambiri zapitazo, choncho tipemphe atsogoleri azipanizi kuti alore mamembala ake kupikisana m’maudindo osiyanasiyana ndikupanga zokomera amalawi,” iwo anatero.

Olemba: George Mkandawire

Related posts

Chakwera engages small-scale traders in Lilongwe

Mayeso Chikhadzula

Bwaila Fistula Centre calls for support to treat more fistula patients

Romeo Umali

VP’s spouse commends SDA women gospel album

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.