Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

Zipani zikusowekera demokalase ndi umodzi, CCAP ya Livingstonia Sinodi yatero

Sinodi ya Livingstonia mu mpingo wa CCAP, pansi pa nthambi yake ya chilungamo ndi mtendere, yati mu zipani zambiri m’dziko muno mulibemo demokalase ndi umodzi.

A Mcbowman Mulagha, mkulu wa nthambiyi, wapeleka chitsanzo chammene zinthu ziliri m’chipani cha Democratic Progressive (DPP) ndi zipani zina.

Posachedwapa, chipani cha DPP chinachotsa ena mwa atsogoleri ake kaamba kophwanya ena mwa malamulo achipanichi.

A Mulagha ati zimenezi zili ndi kuthekera koononga ndale komanso kusokoneza anthu.

“Zipani zandale m’dziko muno ziyambe kutsatira mfundo za demokalase zomwe dziko lino linayamba kutsatira zaka zambiri zapitazo, choncho tipemphe atsogoleri azipanizi kuti alore mamembala ake kupikisana m’maudindo osiyanasiyana ndikupanga zokomera amalawi,” iwo anatero.

Olemba: George Mkandawire

Related posts

Exploring Malawian culture through Sci-Fi: Mombera Rising preview

Romeo Umali

Parliamentarians to convene for CAADP Post Malabo Consultative Meeting

Romeo Umali

MBC JOINS EFFORTS TO SUPPORT CYCLONE FREDDY SURVIVORS

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.