Malawi Broadcasting Corporation
Local News Nkhani Sports Sports

Wanderers idzasankha mphunzitsi watsopano gawo loyamba la super league likatha

Timu ya Mighty Mukuru Wanderers yati idzasakha mphunzitsi watsopano gawo loyamba la super league likatha ndipo yati yemwe akugwirizira udindowu Meke Mwase ali ndi mwayi waukulu otengeratu ntchitoyi.

Mwase akuthandizidwa ndi Bob Mpinganjira kutsatira ndipo adatenga udindowu pambuyo pa kutula pansi udindo kwa Nsazurwimo Ramadan.

Mkulu watimuyi, Panganeni Ndovi, wati aunikira mmene aphunzitsi ogwirizirawa agwilira ntchito gawo loyamba likatha.

Motsogozedwa ndi Mwase, timuyi yapambana masewero ake onse awiri.

Wandereres ili panambala yachitatu mu ligi ndi ma pointi 18.

By Praise Majawa

Related posts

Hilal Africa treats over 3000 muslims in Salima to a feast

Romeo Umali

Trade expert calls for investment in homegrown research

Romeo Umali

Farmers in Kasungu embrace crop diversification for better yields

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.