Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Development Local Local News Nkhani

Ufa othandizira ovutika ndi njala wafika

Gawo loyamba la ufa umene boma lagula wa ndalama zokwana $20 million othandiza anthu amene akhudzidwa ndi njala tsopano wayamba kufika m’dziko muno.

Boma lagula ufawu kudzera ku bungwe la WFP kuchokera m’maiko a South Africa ndi Tanzania.

Mwambo opereka ufawu ku boma wachitika ku Limbe mu mzinda wa Blantyre.

Mlembi wamkulu mu unduna wa zamalimidwe owona za ulimi wanthilira, a Geoffrey Mamba, ndiwo alandira ufawu ku Limbe kuchokera kwa mkulu wa WFP m’dziko muno, a Paul Turnbull.

Anthu okwana 4.4 million ndiwo akuvutika ndi njala ndipo ufawu onse ukwana ma tani 23,000 ndipo ufikira anthu otere kuyambira mawa loweruka, malinga ndi a Mamba.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

We are on towards achieving Malawi 2063 – Chakwera

MBC Online

CHAKWERA TO COMMISSION RENOVATED KAMUZU DAM TOMORROW

McDonald Chiwayula

Mayi Banda akufuna thandizo

Davie Umar
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.