Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Development Local Local News Nkhani

Ufa othandizira ovutika ndi njala wafika

Gawo loyamba la ufa umene boma lagula wa ndalama zokwana $20 million othandiza anthu amene akhudzidwa ndi njala tsopano wayamba kufika m’dziko muno.

Boma lagula ufawu kudzera ku bungwe la WFP kuchokera m’maiko a South Africa ndi Tanzania.

Mwambo opereka ufawu ku boma wachitika ku Limbe mu mzinda wa Blantyre.

Mlembi wamkulu mu unduna wa zamalimidwe owona za ulimi wanthilira, a Geoffrey Mamba, ndiwo alandira ufawu ku Limbe kuchokera kwa mkulu wa WFP m’dziko muno, a Paul Turnbull.

Anthu okwana 4.4 million ndiwo akuvutika ndi njala ndipo ufawu onse ukwana ma tani 23,000 ndipo ufikira anthu otere kuyambira mawa loweruka, malinga ndi a Mamba.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

TEVETA ILIMBIKITSA ACHINYAMATA OMWE ADASIYIRA SUKULU PA NJIRA KULIMBIKIRA NTCHITO ZALUSO

Aisha Amidu

Parliament to hold open session in Dedza

Sothini Ndazi

Veep urges Malawians in Tanzania to invest back home

Arthur Chokhotho
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.