Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Tiyeni titukule dziko – Dr Usi

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr Michael Usi atsimikizira anthu aku Mulanje kuti alandira ngongole zoti achitire bizinesi ndicholinga chotukula miyoyo yawo.

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko linoyu wapemphanso anthu kuti alimbikitse umodzi pa chitukuko.

Iwo ati adindo akuyenera alembe anthu ochita bizinesi zing’onozing’ono mosayang’ana chipani kuti aliyense apindule.

Pa nkhani ya chakudya, Dr Usi ati iwo ali okonzeka kuthandiza anthu achikulire mdera lakwa Golden ndi chakudya pomwenso bungwe la DODMA likhale likuthandiza anthu ndi chakudya, maka omwe alibiletu.

Related posts

Apalasa kuchoka Lilongwe mpaka Blantyre pofuna kutolera K100 million

Romeo Umali

Madinga signs deal with Zambia club

Romeo Umali

Wittika’s murder case adjourned

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.