Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Tiyeni titukule dziko – Dr Usi

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr Michael Usi atsimikizira anthu aku Mulanje kuti alandira ngongole zoti achitire bizinesi ndicholinga chotukula miyoyo yawo.

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko linoyu wapemphanso anthu kuti alimbikitse umodzi pa chitukuko.

Iwo ati adindo akuyenera alembe anthu ochita bizinesi zing’onozing’ono mosayang’ana chipani kuti aliyense apindule.

Pa nkhani ya chakudya, Dr Usi ati iwo ali okonzeka kuthandiza anthu achikulire mdera lakwa Golden ndi chakudya pomwenso bungwe la DODMA likhale likuthandiza anthu ndi chakudya, maka omwe alibiletu.

Related posts

Champiti is CEO of Roads Authority

McDonald Chiwayula

Chinese delegation in Malawi for Xidian Stock Exchange

Yamikani Simtowe

Khothi laimitsa kaye mlandu wa mmwenye ndi mavenda aku Nsungwi

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.