Malawi Broadcasting Corporation
Local News

Mumba wakhazikitsa mfundo zake

Yemwe akupikisana nawo pa mpando wa wachiwiri kwa mtsogoleri wa chipani cha Malawi Congress, MCP, Vitumbiko Mumba wakhazikitsa mfundo zake zokopera nthumwi za ku msonkhano waukulu wa chipanichi ndi cholinga choti akamusankhe pa udindowu.

Mumba wakhazikitsa mfundozi pa msonkhano wa atolankhani ku Mzuzu masana a lamulungu.

Mwa zina, Mumba wati adzatenga gawo lowonetsetsa kuti padzakhale kusiyana pa ntchito za chipani ndi ntchito zotumukira boma la Malawi.

Iye watinso adzaonetsetsa kuti akutumikira ndi kupereka malangizo oyenera kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr. Lazarus Chakwera, yemwenso ndi mtsogoleri wachipani cha MCP.

Chipani cha MCP, chili ndi msonkhano waukulu kuyambira pa 8 mpaka pa 10 mwezi wa mawa, komwe mwazina, chikasankha atsogoleri a komiti yaikulu yoyendetsa chipanichi.

 

Walemba: Musase Cheyo

Related posts

Sanwecka honours pledge to EOY winners

MBC Online

LL Police seizes expired drugs, arrests pharmacists

Mayeso Chikhadzula

The Harps ikondwerera zaka khumi zamaimbidwe ndi makwaya aku Zimbabwe ndi Zambia

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.