Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Dr Usi ati alimbikitsa umodzi

Dr Micheal Usi, amene ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, ati achita zotheka polimbikitsa chipani cha UTM, monga mtsogoleri wachipanichi, kuti chikhale champhamvu.

Iwo ati cholinga chawo ndikukwaniritsa masomphenya a yemwe anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, malemu Dr Saulos Chilima.

Dr Usi anena izi pamene amacheza ndi anthu a kumudzi kwawo kwa Golden kwa mfumu yaikulu Chikumbu m’boma la Mulanje.

Iwo atsimikiziranso anthu a m’boma la Mulanje kuti boma ladzipereka potukula miyoyo yawo, kuphatikizapo kupereka ngongole kwa ochita bizinezi.

 

Related posts

Bullets lift Castel Cup

Romeo Umali

Kampani zamigodi ziyike umwini pa MSE — Misalico

Romeo Umali

Minister warns contractors against shoddy road works

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.