Malawi Broadcasting Corporation
Local News

Tiyeni tigwirizane pokonda dziko – Chaponda

Mtsogoleri  wa zipani zotsutsa kunyumba ya malamulo, a George Chaponda, wati ali ndi chisoni  chifukwa cha imfa ya wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Malemu Dr Saulos Chilima.

Poyankhula ndi MBC ku siwa ku Area 12 mu mzinda wa Lilongwe, a Chaponda anati  Malemu  Dr Chilima akhala akugwira ntchito yotamandika  potumikira a Malawi ndi boma.

Mwazina, a Chaponda apempha a Malawi kuti agwirane manja ndi boma panthawi ya zovutayi ponena kuti maliro sazolowereka.

Akulu akulu a zipani zosiyanasiyana, kuphatikizapo aphungu akunyumba ya malamulo, ali kunyumba ya siwayi.

 

Related posts

DoDMA rescues 90% of food-insecure Malawians

Romeo Umali

Public Pension Funds’ assets valued at K340 billion

Romeo Umali

NICO doubles sponsorship for National Schools Chess League

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.