Apolisi limodzi ndi azachipatala ayamba kunyamula matupi a anthu amene ataya miyoyo yawo pangozi ya ndege imene yagwa chapa Lunjika mu nkhalango ya Chikangawa m’boma la Mzimba.
Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Saulos Chilima pamodzi ndi akuluakulu ena asanu ndi anayi, apezeka atamwalira pa ngoziyi, malinga ndi kutsimikiza kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera pamene amayankhula kwa mtundu wa Malawi.
Pakali pano, matupi a anthuwo akuyembekezeka kutengedwa kuchoka ku nkhalangoyi kupita ku Capital Hill munzinda wa Lilongwe.
Akuluakulu aboma, aphungu aku nyumba ya malamulo komanso makhansala ndi anthu osiyanasiyana ali pamalowa, pamene asilikali a dziko lino akuyesetsa kukhazikitsa bata ndikutsogolera anthu mwadongosolo pa malowa.
Olemba: Jackson Sichali

