Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Tisinthe kaganizidwe a Malawi’

M’busa Yassin Gama, yemwe amatumikira ku mpingo wa Mvama CCAP pansi pa Nkhoma Synod, wapempha aMalawi kuti akhale anthu olimbikira.

Pa ulaliki wawo ochoka m’buku la Yobu pa mapemphero wokumbukira kuti dziko la Malawi lakwanitsa zaka 60,  M’busa Gama anatsindika kuti ndikofunika a Malawi adzikhala ndi umunthu pomadzifunsa kuti Malawi wawo alibwanji.

“Yobu analibe chibwana ngakhale anadwala kwambiri, mabala thupi lonse koma adakanitsitsabe kutukwana Mulungu, zomwe mkazi wake anamuuza,” anatero Abusa Gama.

Pamenepa, iwo anachenjeza aMalawi kuti apewe kutembelera dziko lawo.

Mu uthenga wake, M’busa Esau Banda wa Pentecostal International Christian Centre analimbikitsa aMalawi kufunika kochilimika pokhala anthu a mtendere.

Mwambowu chaka chino ukuchitika ndi mutu woti ‘kuyendera limodzi mochilimika’.

 

Related posts

Zipani zikusowekera demokalase ndi umodzi, CCAP ya Livingstonia Sinodi yatero

MBC Online

Four fishermen arrested for using illegal fishing gear

Alinafe Mlamba

Japan, WFP asainira mgwirizano othandiza dziko la Malawi pavuto la njala

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.