Malawi Broadcasting Corporation
Environment Local Local News

‘TIPEMPHERERE MVULA’ — EAM

Bungwe la atsogoleri a mipingo la Evangelical Association of Malawi (EAM) lati a Malawi ayambe kupempherera mvula kutsatira kugwa kwa ng’amba.

Mlembi wa mkulu wa bungwe la EAM, abusa Francis Mkandawire, ati amene angathe kusala kudya achite chomwecho komanso anthu akhale akupemphera molimba ku nyumba kwawo, malo opembedzera ndi malo ogwira ntchito.

“Mulungu achiritse dziko lathu natipatsa mvula yokwanira ndi kutichotsera mavuto ambiri tikukumana nawo ngati dziko,” a Mkandawire anafotokoza.

M’mbuyomu, nthambi ya za nyengo inati kuyambira mwezi wa February mpakana mwezi wa April, chaka chino, mvula ikhala ikugwa mwa njomba m’madera ambiri m’dziko muno.

Olemba: Romeo Umali

Related posts

ALIMI A MTEDZA APINDULA

Blessings Kanache

PCL achieves 100% profit

Romeo Umali

Popularize international humanitarian law — MDF

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.