Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Tambala Super Cup ayikhazikitsa

Chikho cha mpira wa miyendo cha Tambala Super tsopano achikhazikitsa ndipo adzipikisana ndi matimu ang’onoang’ono a m’boma la Blantyre.

Chikhochi ndi cha ndalama zokwana K10 million zomwe inayikapo ndi kampani ya Amazone Group Limited.

Mkulu wa kampaniyi, a Moses Kunkuyu, anati anaganiza zothandiza chikhochi m’boma lonse la Blantyre popeza iwo ndi nzika yomwe ili ndi mbiri m’madera onse a m’bomali.

Masewero okhazikitsa chikhochi anali apakati pa timu ya Chikuli Young Eagles yomwe inagonjetsa Kumanda All Stars 10-9 pa mapenote atalepherana kugoletsana m’zigawo ziwiri za masewerowa.

Gulu la Black Missionaries komanso Simon ndi Kendal anasangalatsa anthu ndi mayimbidwe pamwambowo.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Chilima, nine others killed in plane crash

MBC Online

MBC appeals for support ahead of EOY

MBC Online

Phyzix set to invade Mzuzu

Kumbukani Phiri
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.