Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Tambala Super Cup ayikhazikitsa

Chikho cha mpira wa miyendo cha Tambala Super tsopano achikhazikitsa ndipo adzipikisana ndi matimu ang’onoang’ono a m’boma la Blantyre.

Chikhochi ndi cha ndalama zokwana K10 million zomwe inayikapo ndi kampani ya Amazone Group Limited.

Mkulu wa kampaniyi, a Moses Kunkuyu, anati anaganiza zothandiza chikhochi m’boma lonse la Blantyre popeza iwo ndi nzika yomwe ili ndi mbiri m’madera onse a m’bomali.

Masewero okhazikitsa chikhochi anali apakati pa timu ya Chikuli Young Eagles yomwe inagonjetsa Kumanda All Stars 10-9 pa mapenote atalepherana kugoletsana m’zigawo ziwiri za masewerowa.

Gulu la Black Missionaries komanso Simon ndi Kendal anasangalatsa anthu ndi mayimbidwe pamwambowo.

 

Related posts

Cameroon replace coach Brys after Eto’o argument

MBC Online

Awiri aphedwa polimbilana ufumu wa Mankhamba

Alinafe Mlamba

CPHIA 2023 TO AMPLIFY AFRICA’S ADOPTION OF DIGITAL HEALTHCARE SYSTEMS

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.