Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Sports Sports

Sitilora kuti atichitse manyazi pakhomo — Mpinganjira

A Bob Mpinganjira, amene ndi mphunzitsi wa timu yampira wa miyendo yadziko lino koma ya achisodzera, wati iwo salola kuti timuyi ichititse anthu manyazi pamene ikhale ikuchita nawo mpikisano wa mayiko anayi omwe ukhale ukuchitika kuyambira lero masana pa bwalo lamasewero la Bingu mumzinda wa Lilongwe.

Lero ndi tsiku lotsegulira masewero kwa achisodzera ndipo ntchito iyamba pamene timu ya Malawi ithambitsane ndi timu ya Zimbabwe.

A Mpinganjira ati awuza anyamata awo kuti asakhale ndi phuma ngati akufuna kuti apambane.

Lachisanu, timu ya Kenya idzasewera ndi Zimbabwe ndipo lamulungu, Malawi idzakumana ndi Kenya amene adzakhale masewero otsiriza.

Malinga ndi malamulo a mpikisanowu, yemwe adzapeze mapointi ochuluka ndi amene adzapambane.

Poyambilira, mu gawo la achisodzera, kumayenereka kukhala mpikisano wa kaphelachoka koma udasintha kaamba kakuti timu ya Zambia ya achisodzera inanena kuti siyichita nawo mpikisanowu pazifukwa zina.

Related posts

Sex enhancers: A deadly gamble for men

MBC Online

Chimwendo to vye for MCP Secretary General position

Mayeso Chikhadzula

Ansah hails Oya

Yamikani Simtowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.