Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Sitalaka ya madalaivala yaonongetsa mkaka wa K120 million

Alimi a ng’ombe za mkaka m’chigawo cha ku m’mwera apempha madalaivala agalimoto zikuluzikulu kuti asiye kunyanyala ntchito chifukwa akutaya mkaka wambiri.

Dzulo lokha, alimiwa ati ataya malita 240 sauzande omwe ndi wa ndalama zokwana pafupifupi K120 million kaamba kakuti galimoto zikuluzikulu zonyamula mkaka sizikuyenda.

Poyankhula pa msonkhano wa olembankhani kwa Bvumbwe m’boma la Thyolo, wapampando wa Farmers Milk Producers Association (FAMPA), a Foster Mulumbe, anati akufuna zokambirana zipitilire pakati pa magulu onse okhudzidwa pa nkhani yonyanyala ntchitoyi uku ntchito zina zonse zikuyenda.

A Mulumbe anati izi zili chomwechi chifukwa alimi awo akusowa mtengo ogwira.

Lachitatu, madalaivalawa amanyanyala ntchito yawo pofuna mabwana awo kuti awakwezere malipilo awo apa mwezi, mwa zina.

Olemba: Geoffrey Chinawa

Related posts

MEC ionjezera masiku m’gawo loyamba la kalembera

Rabson Kondowe

‘Abambo akudzipha kwambiri kaamba kosowa upangiri’

Romeo Umali

Mphenzi yapha asodzi awiri ku Mangochi

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.