Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

‘Palibe chiopsezo chilichonse’

Akuluakulu a malo ogona alendo a Mount Soche munzinda wa Blantyre ati akwanitsa kuzimitsa moto umene unabuka pamalowo.

Malinga ndi mmodzi mwa akuluakuluwo, motowo unabuka ku malo komwe amatayako zinyalala.

Iwo ati motowo sunakhudze malo eni-eni ogona alendo.

Pakadali pano, akuluakuluwo apempha alendo komanso ogwira ntchito amene anathawa pamalopo kuti abwelere, ponena kuti palibe chiwopsezo chilichonse.

 

Related posts

A Ganda ayamikira boma pachitukuko

Romeo Umali

Apolisi agwira ozembetsa makala komanso kulanda galimoto ku Blantyre

Mayeso Chikhadzula

Amumanga atanamiza anthu kuti amachulukitsa ndalama m’matsenga

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.