Malawi Broadcasting Corporation
Development Environment Local Local News Nkhani

DoDMA ilimbikitsa chitukuko cha madzi aukhondo

Anthu opyola 8,000 m’ma boma a Mulanje ndi Phalombe tsopano ali ndi madzi aukhondo kutsatira chitukuko chimene nthambi ya DoDMA yachita m’madera a Kamwendo ndi Misewufolo m’maboma awiriwa.

Ntchito yogawa madzi a m’mipopiyi, amene akuwapopa ndi mphamvu yadzuwa,ayigwira pansi pa Post Cyclone Idai and Kenneth Emergency Recovery and Resilience Project.

Wapampando wa komiti yoyendetsa chitukukochi kwa Kamwendo, a Blessings Mikeas, anati izi zithandiza kwambiri chifukwa madzi am’mijigo mderali amatuluka amchere.

M’modzi wa akuluakulu a Dodma, a Moses Chimphepo, anati zitukuko zotere zachitika m’maboma asanu ndipo anthu a mmaderawa atenge umwini wa chitukukochi kuti chikhalitse.

Kwinanso kumene DoDMA yachita chitukukochi ndi maboma a Chikwawa, Zomba ndi Nsanje.

 

Related posts

Land dispute case adjourned to September

MBC Online

Religious leaders urged to embrace Malawi 2063

Romeo Umali

CRS supports AEJ with K1 million

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.