Malawi Broadcasting Corporation
Development Environment Local Local News Nkhani

DoDMA ilimbikitsa chitukuko cha madzi aukhondo

Anthu opyola 8,000 m’ma boma a Mulanje ndi Phalombe tsopano ali ndi madzi aukhondo kutsatira chitukuko chimene nthambi ya DoDMA yachita m’madera a Kamwendo ndi Misewufolo m’maboma awiriwa.

Ntchito yogawa madzi a m’mipopiyi, amene akuwapopa ndi mphamvu yadzuwa,ayigwira pansi pa Post Cyclone Idai and Kenneth Emergency Recovery and Resilience Project.

Wapampando wa komiti yoyendetsa chitukukochi kwa Kamwendo, a Blessings Mikeas, anati izi zithandiza kwambiri chifukwa madzi am’mijigo mderali amatuluka amchere.

M’modzi wa akuluakulu a Dodma, a Moses Chimphepo, anati zitukuko zotere zachitika m’maboma asanu ndipo anthu a mmaderawa atenge umwini wa chitukukochi kuti chikhalitse.

Kwinanso kumene DoDMA yachita chitukukochi ndi maboma a Chikwawa, Zomba ndi Nsanje.

 

Related posts

National Bank hits K1.1 trillion in market capitalisation on MSE

Rabson Kondowe

‘Musalole andale kukutumani kuti muchite ziwawa’

Romeo Umali

Ireland pledges continued support to Malawi

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.