Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Development Local News Nkhani

TAMA Farmers Trust yayamikira boma pa mitengo yabwino ya fodya

Bungwe la alimi a fodya la TAMA Farmers Trust layamikira mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera poonetsetsa kuti alimi a fodya akugulidwa fodya pa mitengo ya bwino chaka chino.

Mtsogoleri wa bungweli, a Kalima Banda, ayankhula izi ku nyumba ya chifumu mu mzinda wa Lilongwe pamene alimi a fodya a m’bungweli anakumana ndi Dr Chakwera.

A Banda anapempha kuti boma liwathandize pokwanilitsa chiwerengero cha makilogaramu a fodya yemwe ogula akumufuna. Iwo anati ndi zosangalatsa kuona kuti alimi akukondwa ku msikawu kaamba ka mitengo yabwinoyi.

Mwazina, iwo anati anakakonda kuti mtsogoleri wa dziko linoyu apitilize kuthandiza poonetsetsa kuti alimiwa adzilandira ndalama zafodya yemwe agulitsa mmisika ya fodya pakangotha masiku awiri okha.

Related posts

COURT ASKS ACB TO BE TRANSPARENT WITH EVIDENCE IN CHILIMA CORRUPTION CASE

MBC Online

Athana ndi umphawi pokonza sopo

Romeo Umali

Malawians join in Way of the Cross

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.