Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

MEC ikuunika zotsatira za chisankho

Bungwe loyendetsa chisankho m’dziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC) lero likuchita msonkhano ounika momwe zisankho zapadera za pa 23 July, 2024 zinayendera.

Pa msonkhanowo pali mabungwe ndi oimira zipani zandale, mwa ena.

Wapampando wa MEC, Justice Annabel Mtalimanja, wati bungweli linaona kofunika kutero ngati njira imodzi yokonzekera chisankho chimene chichitike chaka cha mawa.

Mwazina, iwo apeza kuti pakufunika mabungwe athandizirepo kumema amayi kuti adzapikisane nawo pa zisankho zikudzazi komanso anthu azindikire zakufunika kolembetsa mukaundula.

Justice Mtalimanja auzanso atolankhani kuti bungweli silichitanso zisankho zina zapadera kuti opikisana akonzekere chisankho cha 2025.

Related posts

Nkhanza za m’banja zachuluka m’boma la Balaka – Apolisi

Rabson Kondowe

Makolo asiya mwana pa golosale

Blessings Kanache

Boma ligula PREP ochuluka chaka chamawa

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.