Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

MEC ikuunika zotsatira za chisankho

Bungwe loyendetsa chisankho m’dziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC) lero likuchita msonkhano ounika momwe zisankho zapadera za pa 23 July, 2024 zinayendera.

Pa msonkhanowo pali mabungwe ndi oimira zipani zandale, mwa ena.

Wapampando wa MEC, Justice Annabel Mtalimanja, wati bungweli linaona kofunika kutero ngati njira imodzi yokonzekera chisankho chimene chichitike chaka cha mawa.

Mwazina, iwo apeza kuti pakufunika mabungwe athandizirepo kumema amayi kuti adzapikisane nawo pa zisankho zikudzazi komanso anthu azindikire zakufunika kolembetsa mukaundula.

Justice Mtalimanja auzanso atolankhani kuti bungweli silichitanso zisankho zina zapadera kuti opikisana akonzekere chisankho cha 2025.

Related posts

Japan, WFP asainira mgwirizano othandiza dziko la Malawi pavuto la njala

Rabson Kondowe

T/A Amidu alowa mmanda

Rabson Kondowe

NRB yalemba anthu opitilira 1.5 miliyoni mu ndondomeko yakalembera

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.