Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Scorchers lero imwemwetera

Atsikana amene amasewera mpira wamiyendo mu timu yadziko lino ya Scorchers adzuka ndinkhope zowala chifukwa lero boma likuyembekezeka kukwaniritsa zimene mtsogoleri wadziko lino, Dr Lazarus Chakwera, analonjeza kuti apatsidwa malo chifukwa chotenga chikho cha COSAFA m’dziko la South Africa.

Unduna wa za malo ukuyembekezeka kugawa malo kwa aliyense wa osewerawa, ndipo malowa ndi okula milingo 35 mulitali ndi milingo 25 mulifupi ku Area 45 mu mzinda wa Lilongwe.

Malinga ndi akuluakulu ku unduna wa za masewero, ntchitoyi ikuyembekezeka kuyamba mma 8:30 mmawa uno.

Related posts

Chakwera akumana ndi Papa Francis

Blessings Kanache

Khosolo ya Lilongwe yakhazikitsa komiti yoona za bata ndi mtendere

Rabson Kondowe

Ndondomeko ya mphamvu ku anthu yachiwiri akuikhazikitsa ku Lilongwe

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.