Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Ntchito yojambula msewu wa Makanjira-Mangochi igwiridwa mwachangu

A Saudi Fund for Development ati afulumizitsa ntchito yojambula msewu wa Makanjira ku Mangochi kuti ntchito yomanga msewuwu iyambe mwachangu.

Izi akuti zikutengera chidwi chomwe boma la Malawi likuonetsa pofuna kuthandiza mayendedwe a anthu aku Makanjira.

Wachiwiri kwa mkulu wa Saudi Fund for Development, a Faisal Al-Kahtani, amalankhula ii mu mzinda wa Washington DC pamene anakumana ndi nduna ya zachuma, a Simplex Chithyola Banda, amene akuchita nawo msonkhano waukulu wa zachuma padziko lonse.

A Chithyola Banda akuti boma laika chidwi chonse kuti nsewu umenewu ukonzedwe poti kwa nthawi yaitali anthu akhala akudikira za nseu umenewu kuti ukhale waphula.

Related posts

‘Nyimbo zotchyakuka zikhoza kuchepetsa imfa zodzipha’

Romeo Umali

ZAMBIRI MWA ZIMENE A CHAKWERA ANALONJEZA MU SONA YA 2023 ZACHITIKA – NDUNA

MBC Online

A Kasambara awayika m’manda pa mwambo wachisilikali

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.