Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Ntchito yojambula msewu wa Makanjira-Mangochi igwiridwa mwachangu

A Saudi Fund for Development ati afulumizitsa ntchito yojambula msewu wa Makanjira ku Mangochi kuti ntchito yomanga msewuwu iyambe mwachangu.

Izi akuti zikutengera chidwi chomwe boma la Malawi likuonetsa pofuna kuthandiza mayendedwe a anthu aku Makanjira.

Wachiwiri kwa mkulu wa Saudi Fund for Development, a Faisal Al-Kahtani, amalankhula ii mu mzinda wa Washington DC pamene anakumana ndi nduna ya zachuma, a Simplex Chithyola Banda, amene akuchita nawo msonkhano waukulu wa zachuma padziko lonse.

A Chithyola Banda akuti boma laika chidwi chonse kuti nsewu umenewu ukonzedwe poti kwa nthawi yaitali anthu akhala akudikira za nseu umenewu kuti ukhale waphula.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Chionetsero cha kanema chilipo mu November

Austin Fukula

Masewero a Darts m’chigawo chapakati apeza thandizo

Foster Maulidi

Dr Usi akhumudwa ndi kuonongwedwa kwa CDF

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.