Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Ntchito yojambula msewu wa Makanjira-Mangochi igwiridwa mwachangu

A Saudi Fund for Development ati afulumizitsa ntchito yojambula msewu wa Makanjira ku Mangochi kuti ntchito yomanga msewuwu iyambe mwachangu.

Izi akuti zikutengera chidwi chomwe boma la Malawi likuonetsa pofuna kuthandiza mayendedwe a anthu aku Makanjira.

Wachiwiri kwa mkulu wa Saudi Fund for Development, a Faisal Al-Kahtani, amalankhula ii mu mzinda wa Washington DC pamene anakumana ndi nduna ya zachuma, a Simplex Chithyola Banda, amene akuchita nawo msonkhano waukulu wa zachuma padziko lonse.

A Chithyola Banda akuti boma laika chidwi chonse kuti nsewu umenewu ukonzedwe poti kwa nthawi yaitali anthu akhala akudikira za nseu umenewu kuti ukhale waphula.

Related posts

Tifikireni nthawi zonse -OPC

MBC Online

Atsiriza kufufuza za imfa ya anthu asanu ku Blantyre

Blessings Kanache

‘A Chakwera ataya kholo mu uzimu’

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.