Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Ntchito yojambula msewu wa Makanjira-Mangochi igwiridwa mwachangu

A Saudi Fund for Development ati afulumizitsa ntchito yojambula msewu wa Makanjira ku Mangochi kuti ntchito yomanga msewuwu iyambe mwachangu.

Izi akuti zikutengera chidwi chomwe boma la Malawi likuonetsa pofuna kuthandiza mayendedwe a anthu aku Makanjira.

Wachiwiri kwa mkulu wa Saudi Fund for Development, a Faisal Al-Kahtani, amalankhula ii mu mzinda wa Washington DC pamene anakumana ndi nduna ya zachuma, a Simplex Chithyola Banda, amene akuchita nawo msonkhano waukulu wa zachuma padziko lonse.

A Chithyola Banda akuti boma laika chidwi chonse kuti nsewu umenewu ukonzedwe poti kwa nthawi yaitali anthu akhala akudikira za nseu umenewu kuti ukhale waphula.

Related posts

Blue Eagles yatsala ndi ma poyinsi atatu kuti ibwerere mu super league

Rabson Kondowe

‘Tiganizireni poonjezera ndalama za mtukula pakhomo’

MBC Online

Ntchito zaluso la manja zasintha miyoyo

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.