Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ndondomeko ya mphamvu ku anthu yachiwiri akuikhazikitsa ku Lilongwe

Unduna woona maboma ang’ono ang’ono, umodzi komanso chikhalidwe mmawa uno ukukhazikitsa ndondomeko yachiwiri ya mphamvu ku anthu munzinda wa Lilongwe.

Mlozo wachiwiri-wu akonzamo zovuta zina zimene mlozo wakale  woyamba wa 1998 unali nawo zomwe  zimalepheretsa anthu kutukuka, kutenga mbali muzochitika zambiri zaboma komanso kuthandizidwa moyenera ndi makhonsolo osiyanasiyana a boma kuti mzika zikhale ndi mphamvu pochita zinthu.

Pamwambowu makhonsolo, adindo aboma, a  World Banki ndi ena  akhalanso ndi mwayi wophunzira momwe  ndondomeko yoyamba yathandizira dziko lino kudzera mu mloza wakalewo.

Nduna yoona maboma ang’ono, a Richard Chimwendo Banda, ndiwo akhazikitse mlozo wachiwiriwu.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Four arrested for armed robbery in Nkhata Bay

MBC Online

K15 Million ndiyomwe ikufunika kuthandizira Peter Mlangeni

Paul Mlowoka

Mphunzitsi amumanga ataba ndalama za mayeso

Charles Pensulo
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.