Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ndondomeko ya mphamvu ku anthu yachiwiri akuikhazikitsa ku Lilongwe

Unduna woona maboma ang’ono ang’ono, umodzi komanso chikhalidwe mmawa uno ukukhazikitsa ndondomeko yachiwiri ya mphamvu ku anthu munzinda wa Lilongwe.

Mlozo wachiwiri-wu akonzamo zovuta zina zimene mlozo wakale  woyamba wa 1998 unali nawo zomwe  zimalepheretsa anthu kutukuka, kutenga mbali muzochitika zambiri zaboma komanso kuthandizidwa moyenera ndi makhonsolo osiyanasiyana a boma kuti mzika zikhale ndi mphamvu pochita zinthu.

Pamwambowu makhonsolo, adindo aboma, a  World Banki ndi ena  akhalanso ndi mwayi wophunzira momwe  ndondomeko yoyamba yathandizira dziko lino kudzera mu mloza wakalewo.

Nduna yoona maboma ang’ono, a Richard Chimwendo Banda, ndiwo akhazikitse mlozo wachiwiriwu.

Related posts

Zomba farmers on a learning visit in Nkhotakota

Romeo Umali

Matola condemns vandalism of power line

Mayeso Chikhadzula

Norwegian govt committed to ensuring Malawians register for votes

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.