Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Business Development Local Local News

Salima Sugar yayambanso kupanga Shuga

Kampani ya Salima Sugar yayambiranso kupanga Shuga pamene nyengo yopumira yatha tsopano.

Nyengoyi imakhalapo chaka chilichonse kuyambira mwezi ya November mpaka April.

A Sosten Gwengwe, omwe ndi nduna ya zamalonda, alamula kampaniyi kuti iwonetsetse kuti Shuga wawo akupezeka pa msika ngati njira imodzi yothana ndi vuto lakusowa kwa katunduyi.

Kampaniyi imapanga shuga wochuluka 125 metric tons patsiku, yemwe ndi wa ndalama zokwana K225 million.

Uyu akhala sugar oyamba kupangidwa pa kampaniyi ndi a Malawi chisiyileni mgwirizano ndi kampani ya AUM Sugar and Allied Limited yaku India.

#MBCDigital
#Manthu

 

Related posts

A Malawi First sachitanso zionetsero zotsutsana ndi chizindikiro cha tax stamp

McDonald Chiwayula

MCP ikufuna zipani zidzichita misonkhano mwaufulu

Rabson Kondowe

CS-EPWP participants hail programme for providing income source

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.