Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

President Chakwera apitiliza ulendo m’chigawi cha ku m’mawa

Popitiriza ndi ulendo wake m’chigawo chakummawa kwa dziko lino, Prezidenti Dr Lazarus Chakwera lero ayendera chitukuko chosiyanasiyana m’boma la Balaka.

Mtsogoleri wadziko linoyu ayendera Demeter Mega Farm ku Nkaya ndipo kenaka akayendera fakitale yopanga cement ya kampani ya Portland kwa mfumu yayikulu Nsamala ku Balaka komweko.

Kenaka, Dr Chakwera akakhala mlendo olemekezeka pamwambo okondwelera kuti bungwe logawa ngongole la NEEF tsopano lakwanitsa kugawa ngongole zokwana K1 billion.

Mwambowu ukuchitikira pa bwalo la zamasewero la Balaka.

 

Related posts

MBC BOARD CHAIR CHALLENGES STAFF ON QUALITY PROGRAMMING

MBC Online

Boma ligula PREP ochuluka chaka chamawa

Rabson Kondowe

PP’s convention set

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.