Malawi Broadcasting Corporation
Africa Entertainment Entertainment International Music News Nkhani

Awiri ali mwakayakaya ku chipatala

Oyimba wamkazi Puleng Phoofolo pamodzi ndi munthu wina amene amayendetsa galimoto ali m’chipatala cha Boitumelo m’dziko la South Africa kutsatira ngozi imene achita dzulo masana ku Free State m’dzikolo.

Oyimba odziwika bwino Malome Vector, Lizwi Wokuqala pamodzi ndi katswiri ojambula makanema Da Mos ndiwo afa pangoziyi.

Koma malipoti a ku South Africa akutsutsa kuti oyimba Wave Ryder ndi Ntate Stunna anali anali nawo pangoziyo.

Anthu asanuwa anali pa ulendo okajambula kanema wa nyimbo yawo yatsopano pomwe galimoto limene anakwera linaphulika tayala ndipo linakaombana ndi galimoto lamtundu wa truck.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Jordan Kowet wins St. Patrick’s mental Maths competition

Chisomo Break

MITC urge producers to increase value-added exports

Aisha Amidu

Veep returns

Beatrice Mwape
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.