Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Religion

‘Pewani kufalitsa nkhani zabodza’

Akuluakulu a Religious Leaders Organisation apempha atsogoleri a mipingo m’dziko muno kuti achepetse kuyankhula kapena kuyika ndemanga pa nkhani zomwe zingayipitse mbiri komanso utsogoleri wadziko la Malawi.

Adindo a bungweli amayankhula izi mu nzinda wa Lilongwe pamwambo wa mapemphero omwe anachititsa popemphelera utsogoleri wa dziko lino komanso mavuto amene akuchitika monga imfa, ngozi zogwa mwadzidzidzi ndi kugwiritsa ntchito makina a internet molakwika.

A Muhammed Chindamba, amene ndi mkulu wa bungweli, apempha anthu ndi atsogoleri a mipingo kuti apewe kuyankhula ndi kufalitsa nkhani zopanda umboni.

Iwo anati kupanda kutero, zikhoza kusokoneza umodzi ndi mtendere wa dziko lino.

M’modzi mwa adindo a bungweli, m’busa Brian Nyirenda, anaonjezerapo kuti zimenezi zitha kubwezeretsa m’mbuyo ntchito za chitukuko m’dziko muno ndipo a Malawi akhale ogwirizana pofunira zabwino dziko lawo pamene likudutsa m’mikwingirima.

 

Related posts

FUTURELIFE- NOW! AWARDS BEST STUDENTS IN DEDZA

MBC Online

Kamwendo is a Nomad’s striker

Romeo Umali

Zavutaso ku COSAFA

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.