Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Religion

‘Pewani kufalitsa nkhani zabodza’

Akuluakulu a Religious Leaders Organisation apempha atsogoleri a mipingo m’dziko muno kuti achepetse kuyankhula kapena kuyika ndemanga pa nkhani zomwe zingayipitse mbiri komanso utsogoleri wadziko la Malawi.

Adindo a bungweli amayankhula izi mu nzinda wa Lilongwe pamwambo wa mapemphero omwe anachititsa popemphelera utsogoleri wa dziko lino komanso mavuto amene akuchitika monga imfa, ngozi zogwa mwadzidzidzi ndi kugwiritsa ntchito makina a internet molakwika.

A Muhammed Chindamba, amene ndi mkulu wa bungweli, apempha anthu ndi atsogoleri a mipingo kuti apewe kuyankhula ndi kufalitsa nkhani zopanda umboni.

Iwo anati kupanda kutero, zikhoza kusokoneza umodzi ndi mtendere wa dziko lino.

M’modzi mwa adindo a bungweli, m’busa Brian Nyirenda, anaonjezerapo kuti zimenezi zitha kubwezeretsa m’mbuyo ntchito za chitukuko m’dziko muno ndipo a Malawi akhale ogwirizana pofunira zabwino dziko lawo pamene likudutsa m’mikwingirima.

 

Related posts

UNIMA drills writers on creative writing

Rabson Kondowe

MCP gears for 2025 Elections

Mayeso Chikhadzula

Dedza District Council supports police visibility with new unit

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.