Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Awamanga ataba mabisiketi ku kampani ya Universal

Apolisi ku Area 36 ku Lilongwe amanga anthu atatu powaganizira kuti anathyola ndikuba katundu wa mnyumba wa ndalama pafupifupi K7.5 million, kenako usiku womwewo anakaba mabisiketi ku kampani ya Universal Industries.

Mneneri wapolisi ku Lilongwe, Hastings Chigalu, wati anthuwo ndi Yamikani Sosten wazaka 32 yemwe amadziwikanso kuti “Short”, Martin Lukiya wazaka 38 ndi  Dominic Gilbert wazaka 35.

A Chigalu ati apolisi anapita kunyumba kwa mbavazo akuluakulu a kampani ya Universal Industries atakapereka lipoti ku ofesi yawo.

Atafika kunyumbako, apolisiwo anapezanso katundu wina wamnyumba yemwe mbavazo zinaulula kuti zinakaba ku Area 36 ndipo mwini nyumbayo anali asanadziwe kuti kunyumba kwake kwabedwa, ngakhale panali patadutsa tsiku limodzi.

A Chigalu anatsimikiza kuti mwini nyumbayo sanadziwedi kanthu mpaka pomwe apolisiwo anapita kukamudziwitsa kuti waberedwa.

Related posts

NEEF tiyithandize — Dimba

Romeo Umali

MUBAS champions research and innovation for Malawi 2063

Rabson Kondowe

Amumanga ataba mbendera yadziko

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.