Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Religion

Parish ya Nzama yakwana zaka 125

Kuli chikondwelero ku Parish ya mpingo wa Katolika ya Nzama m’boma la Ntcheu pamene akukhazikitsa nyengo yokondwelera kuti papita zaka 125 chiyikhazikitsireni.

Malinga ndi Bambo Godno Chinkanda a pa Parishiyi, malowa, amene ali m’dera la T/A Mpando, ndi ofunikira kwambiri mu mbiri ya a Katolika komanso dziko la Malawi.

Iwo ati, mwazina, kumeneku ndi kumene kunayambira sukulu ya ukachenjede ya katolika m’chaka cha 1902.

Ma mishonale a chi katolika anafika ku Nzama m’chaka cha 1901 pa 25 July.

Iwo ati chikondwelerochi chidzafika pa chimake m’chaka cha 2026.

 

Related posts

Dr Chakwera akumana ndi atsogoleri azipembedzo

Romeo Umali

CHAKWERA ARRIVES IN DRC

MBC Online

Kalindo back in court for the firearm acquisition case

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.