Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Religion

Parish ya Nzama yakwana zaka 125

Kuli chikondwelero ku Parish ya mpingo wa Katolika ya Nzama m’boma la Ntcheu pamene akukhazikitsa nyengo yokondwelera kuti papita zaka 125 chiyikhazikitsireni.

Malinga ndi Bambo Godno Chinkanda a pa Parishiyi, malowa, amene ali m’dera la T/A Mpando, ndi ofunikira kwambiri mu mbiri ya a Katolika komanso dziko la Malawi.

Iwo ati, mwazina, kumeneku ndi kumene kunayambira sukulu ya ukachenjede ya katolika m’chaka cha 1902.

Ma mishonale a chi katolika anafika ku Nzama m’chaka cha 1901 pa 25 July.

Iwo ati chikondwelerochi chidzafika pa chimake m’chaka cha 2026.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Malawi prepares e-justice era

MBC Online

Msilikali Sacco AGM approves K156M dividends payout

Yamikani Simutowe

MBC for continued collaboration with DIOs

Timothy Kateta
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.