Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Technology

Ntchito za ICT ndi zandalama — Kunkuyu

Nduna ya Zofalitsa nkhani, a Moses Kunkuyu, yayamika m’modzi mwa anthu ochita malonda pa luso la makono (ICT), a Wisely Phiri, amene ndi mwini wake wa Sparc Systems, kaamba komanga nyumba ya makono kwambiri munzinda wa Lilongwe.

A Kunkuyu ati zimene achita a Phiri ndi umboni okuti mu ntchito za ICT muli ndalama zimene zingathandize pa chitukuko cha dziko lino.

Iwo anati nthawi zambiri a Malawi amaziyang’anira pansi m’malo mochita zinthu zothandiza kutchukitsa dziko lino.

A Phiri anati alinso ndi mapulani omanga sukulu yophunzitsa ICT ku Blantyre komanso mayiko a Zambia ndi Mozambique.

Iwo apempha boma kuti lidzipereka ma contract ambiri kwa a business achi Malawi pofuna kulimbikitsa aMalawiwo pa ntchito zokweza dziko lino.

Sparc Systems Limited adayikhazikitsa 2013 ndipo ili ndi ofesi kuno ku Malawi, Zambia ndi Rwanda.

 

Related posts

Dedza District Council calls off council meeting

Romeo Umali

PAC urges unity in fight against smuggling

McDonald Chiwayula

CHAKWERA ATTENDS UNGA OPENING

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.