Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Technology

Ntchito za ICT ndi zandalama — Kunkuyu

Nduna ya Zofalitsa nkhani, a Moses Kunkuyu, yayamika m’modzi mwa anthu ochita malonda pa luso la makono (ICT), a Wisely Phiri, amene ndi mwini wake wa Sparc Systems, kaamba komanga nyumba ya makono kwambiri munzinda wa Lilongwe.

A Kunkuyu ati zimene achita a Phiri ndi umboni okuti mu ntchito za ICT muli ndalama zimene zingathandize pa chitukuko cha dziko lino.

Iwo anati nthawi zambiri a Malawi amaziyang’anira pansi m’malo mochita zinthu zothandiza kutchukitsa dziko lino.

A Phiri anati alinso ndi mapulani omanga sukulu yophunzitsa ICT ku Blantyre komanso mayiko a Zambia ndi Mozambique.

Iwo apempha boma kuti lidzipereka ma contract ambiri kwa a business achi Malawi pofuna kulimbikitsa aMalawiwo pa ntchito zokweza dziko lino.

Sparc Systems Limited adayikhazikitsa 2013 ndipo ili ndi ofesi kuno ku Malawi, Zambia ndi Rwanda.

 

Related posts

‘Regular screening vital in combating breast cancer’

Rabson Kondowe

Former inmates are part of the community – CHREAA

MBC Online

First Lady urges women to lead in praying for Malawi’s progress

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.