Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Nkhanza za m’banja zachuluka m’boma la Balaka – Apolisi

Apolisi m’boma la Balaka  adandaula ndi kukwera kwa chiwerengero cha milandu yokhuza nkhanza m’mawanja m’bomalo. 

Malinga ndi wofalitsa nkhani za apolisi m’bomalo, a Gladson M’bumpha, kuchokera mwezi wa January kufika mwezi wa June chaka chino m’bomalo alandira milandu yoposa 280  poyerekeza ndi milandu 180 mu nthawi ngati yomweyi chaka chatha.

Pakadali pano mlembi wamkulu wa bungwe lachipemebezo la Malawi Council of Churches (MCC), m’busa Alemekezeke Phiri wati mipingo mdziko muno ili ndikuthekera kothandiza kuchepetsa nkhanza m’banja.

Mwa zina m’busa Phiri wati  nchifukwa chake bungwe la MCC lakhala likuchititsa maphunziro m’maboma ena m’dziko muno kuphatikizapo la Balaka komwe akuphunzitsa atsogoleri a mipingo kuti mu ulaliki wawo adzikambamonso nkhani zokhudza kuipa kwa nkhanza mmabanja.

 

Olemba: Alufeyo Liyaya

Related posts

Mtsikana wa zaka 17 wapha mwana

Romeo Umali

Kamberembere wobera anthu kudzera pa masamba a mchezo amumanga

Romeo Umali

President Chakwera back in the Capital City

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.