Bungwe la National Economic Empowerment Fund (NEEF) lakhazikitsa ntchito ya ngongole yaza ulimi wa mthilira m’chigawo cha m’mphepete mwa nyanja.
Mkulu wabungweli, a Humphrey Mdyetseni, ati cholinga cha ntchitoyi ndi kufuna kuthana ndi vuto la njala m’dziko muno.
A Mdyetseni ati ndi khumbo la mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, kuti mitengo ya chimanga ikhale yokhazikika ndipo ndi chifukwa chake akulimbikitsa ulimi wa mthilira.
Iwo ati anthu akhala akulandira ngongolezi kufikira nyengo ya ulimi wodalira mvula itafikanso.
Mkulu waza ulimi m’boma la Salima, a Eniford Kanyimbo, wapempha alimi omwe apeze zipangizo za ulimizi kuti akumbukire kubweza ngongole akakolola zinthu zawo m’mwezi wa August chaka chino.
Kudzera ku ntchitoyi, anthu omwe apindule ndi oposa 200,000 ndipo adziwapatsa mbewu, fetereza komanso makina othililira oyendera mphamvu ya dzuwa.
Chaka chatha, bungwe la NEEF lidapereka ngongole yokwana K10.2 billion yothandizira ulimi wa mthilira ndipo anthu oposa 5,000 ndi omwe adapindula.