Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Mwana wamwalira makolo ake atakana kumutengera kuchipatala

Apolisi ku Zomba amanga Frederick Masiku wazaka 46 ndi mkazi wake Fasilen Golosi wazaka 38 chifukwa chokaniza kutengera mwana wawo kuchipatala chifukwa cha chipembedzo.

Mneneri wapolisi ku Zomba Patricia Sipiliano wati mwana wa banjalo wazaka zisanu anadwala mutu. Kenako banjalo linayamba kupemphelera mwanayo koma mwatsoka anamwalira.

Banjali ndi la mmudzi wa Ramusi 2 Mfumu yaikulu Ramusi ku Zomba.

Related posts

‘Pewani kufalitsa nkhani zabodza’

Romeo Umali

Munthu mmodzi wavulala modetsa nkhawa pa ngozi ya sitima

Romeo Umali

NGORA yati K1BN ithandiza mabungwe awo kudzidalira

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.