Osewera wakale watimu ya Silver Strikers Mike Robert, wamwalira kamba kavuto la impso kuchipatala cha Kamuzu Central munzinda wa Lilongwe.
Mng’ono wake wa Mike, Jacob,yemwe amasewera mutimu ya Blue Eagles, wati mkulu wakeyu wakhala akuvutika ndi nthenda ya impso kwa nthawi yayitali.
Jacob wati Mike pakatipa anadwalanso malungo aakulu amene anathamangira ku ubongo ndipo lero chamma 4 koloko kumadzuloku ndi pamene wamwalira.
Jacob watiuza kuti padakali pano dongosolo la mwambo wa maliro silinadziwike.
Mike anakhalako mtsogoleri wa osewera atimu ya Silver ndipo amachokera m’boma la Dowa.
Olemba : Praise Majawa