Malawi Broadcasting Corporation
Local News Nkhani

Munthu mmodzi wavulala modetsa nkhawa pa ngozi ya sitima

Munthu mmodzi wavulala modetsa nkhawa pa ngozi ya sitima ku Blantyre mu njanji ya Magalasi – Nyambadwe – kudutsa ku Chapima.

Ofalitsankhani za polisi ya Ndirande, a Maxwell Jailosi, ati adakafufuzabe za nkhaniyi ndipo a kampani ya CEAR, omwe ndi eni sitimayi, sanapezeke kuti ayankhulepo pa nkhaniyi.

Koma malinga ndi anthu amene akuti anawona ngoziyi ikuchitika, munthuyu anadumpha mu sitimayi, yomwe inali ikuyenda, pamene ena akuti amayesera kukwera sitimayi ikuyenda.

Munthuyu akulandira thandizo la mankhwala pa chipatala cha QECH.

Olemba: Blessings Cheleuka

Related posts

Mozambique-Malawi project ready by 2025 – ESCOM

Rabson Kondowe

MoH proposes mandatory use of ID, birth certificates in accessing health services

Rabson Kondowe

MEC for smooth elections

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.