Malawi Broadcasting Corporation
Local News Nkhani Religion

Atsogoleri azipembedzo alimbikitsa bata

Bungwe la atsogoleri azipembedzo zosiyanasiyana m’dziko muno la Religious Leaders Organisation lapempha anthu kuti adzikhala mwabata nthawi zonse ndi kulemekeza atsogoleri adziko.

Mtsogoleri wabungweli, Sheikh Muhammad Chindamba, walankhula izi ku Lilongwe pamsonkhano omwe anakonza opemphelera dziko komanso kusankha adindo a abungweli.

Iwo ati ndizomvetsa chisoni kuti atsogoleri azipembedzo ena, omwe ntchito yawo ndikukhazikitsa bata ndi mtendere, akumayankhula mobweretsa chisokonezo, maka pamasamba a mchezo.

Iwo ati ndikofunika mtsogoleri wachipembedzo aliyense awonetsetse kuti akulimbikitsa umodzi ndi mtendere.

 

Related posts

President Chakwera to meet Rotary International president

Rabson Kondowe

NCHE, APUMA push for closer collaboration on standards

McDonald Chiwayula

Philanthropist pumps in K10 million in Neno Football and Netball Leagues

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.