Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Mukatengera chipani njala ikusautsani, watero Kalitendere

Phungu wanyumba ya malamulo wa dera la kumpoto chakummawa kwa boma la Machinga, Ajilu Kalitendere, walangiza anthu a m’dera lake kuti alandire ufa umene boma likugawa kutsatira njala imene yagwa m’dziko muno.

A Kalitendere amayankhula ku Nainunje kwa mfumu yaikulu Kapoloma ku Machinga kumene bungwe loona za ngozi zogwa mwadzidzidzi la DoDMA lagawa matumba a ufa okwana 1,254 kwa omwe akhudzidwa ndi njala.

Iye anauza anthuwo kuti akatengera zakuti MCP ndiyomwe ikugawa ufawo pomwe iwo ndi achipani china, afa ndi njala.

Wolemba: Davie Umar

Related posts

Ligi ipitilira mwezi ukaooneka — Classic U-20 Volleyball

Romeo Umali

‘Ndondomeko ya NEEF isintha miyoyo ya ambiri’ — Chakwera

Alinafe Mlamba

Apolisi amanga mlonda pomuganizira kuti anaba

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.