Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

‘Timanga wina aliyense oyambitsa ziwawa zandale’

Mkulu wa apolisi m’dziko muno, a Merlyne Yolamu, wachenjeza kuti apolisi athana ndi wina aliyense oyambitsa ziwawa panthawi imene zokonzekera zachisankho zili mkati.

A Yolamu apereka chenjezoli pa msonkhano opereka uthenga olimbana ndi nkhanza zosiyanasiyana, omwe unachitikira m’boma la Mzimba pa Jenda.

“Ndichenjeze pano kuti timanga wina aliyense oyambitsa zisokonezo nthawi ino, lolani wina aliyense apange msonkhano wake mwaufulu posazulirana mbendera kapena kemenyana,” anatero a Yolamu.

Iwo anati a Malawi ndi amodzi ngakhale amasiyana zipani kotero anthu sakuyenera kusankhana.

Olemba: Henry Haukeya

Related posts

WE ARE BACK WITH MBC ENTERTAINERS OF THE YEAR! STAY TUNED THIS EVENING!

McDonald Chiwayula

Ogonana okhaokha chigamulo mawa

Rabson Kondowe

FEDOMA talks inclusion in natural disaster management

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.