Malawi Broadcasting Corporation
Business Local Local News Nkhani

Mpinganjira apereka mpamba wa malonda kwa achinyamata 30

Achinyamata makumi atatu lero akuyembekezera kupata mwayi wa mpamba oyambira malonda okwana K1 million aliyense kuchokera kwa mayi Triephornia Mpinganjira ku BICC mu mzinda wa Lilongwe.

Izi zili pansi pa ndondomeko yomwe adakhazikitsa yothandiza achinyamatawa yotchedwa Kuthandiza Omwe Alibe Kuthekera Kupita Patsogolo.

Zokonzekera mwambowu zili m’chimake ndipo mayi Mpinganjira komanso Dr Thomson Mpinganjira ndi amene atsogolere mwambowu.

Pachiyambi, mayi Mpinganjira adayika ndalama zokwana K18 million pofuna kuthandiza achinyamata 18 koma chiwerengerochi chidakwera kufika pa achinyamata 34 pomwe nawo Dr Thomson Mpinganjira adaonjezera K14 million pomwe kampani ya Credible Investments Limited idathandizanso ndondomekoyi ndi K2 million.

Akuluakulu ena ochita malonda monga Dr Napoleon Dzombe komanso mkulu wa kampani ya Imosys, a Mayamiko Nkoloma akuyembekezeka kukhalanawo ndi kuyankhula ndi achinyamatawa pamwambowu

Mayi Triephornia Mpinganjira adakhazikitsa ndondomekoyi pa 16 April chaka chino ndipo achinyamata anayi oyamba adalandira kale mpambawu.

 

Related posts

TNM appreciates role of bankers in Malawi

Alinafe Mlamba

Chakwera to swear in Deputy Chief Justice

McDonald Chiwayula

CHAKWERA CALLS FOR COLLECTIVE APPROACH TO DEVELOP MALAWI

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.