Malawi Broadcasting Corporation
Crime Education Local Local News Nkhani

Mphunzitsi amumanga pomuganizira kuti wagwilira ophunzira

Apolisi ku Namwera m’boma la Mangochi atsekera m’chitokosi a Nelson Lipenga azaka 49 zakubadwa powaganizira kuti akhala akugwilira ophunzira wa zaka 15 wa Standard 8 pasukulu ya pulaimale ya Mama Khadija, yomwe ndi ya atsikana okhaokha.

Ofalitsa Nkhani za Polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daudi, watsimikiza nkhaniyi ndipo wati oyang’anira atsikanawa ndiye adawapezelera anthuwa nthawi yamadzulo atatsekerana m’chipinda china ndipo panthawiyi mtsikanayu amayenera kukhala m’chipinda chowerengela limodzi ndi amzake.

Nkhaniyi itapita ku Polisi, mtsikanayu anaulula kuti anthuwa adayamba kugonana chaka chatha iyeyu ali Standard 7.

A Lipenga awatsegulira mulandu ochita zadama ndi mwana ndipo akaonekera ku khoti apolisi akatsiriza kufufuza za nkhaniyi.

 

Related posts

Finance Minister urges Malawians to support economic transformation vision

Rabson Kondowe

Girl killed in Nkhata Bay road accident

Romeo Umali

Malawi needs homegrown solutions, says Finance Minister at ECAMA Conference

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.