Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Mphenzi yapha asodzi awiri ku Mangochi

Asodzi awiri afa panyanja ya Malawi mphenzi itawaomba, malinga ndi ofalitsa nkhani pa polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daudi.

A Daudi ati ngoziyi yachitika mdera la mfumu Moto mdera la mfumu yaikulu Namabvi.

“Tamvetsedwa kuti asodziwa anali panyanja kugwira ntchito yawo monga mwamasiku onse koma mwadzidzi kunayamba mphepo ya mwera ndi mvula yamphamvu yophatikizana ndi mphenzi yomwe inaomba bwato lawo,” a Daudi anatero.

Iwo anatinso chifukwa cha mphamvu za nyetsi ya mphenziyo, asodziwo anagwera m’madzi ndipo matupi awo apezeka atatentheka kwambiri.

 

Related posts

Prezidenti Chakwera acheza ndi anthu pa Nanyumbu ku Machinga

Rabson Kondowe

DAPP trains 96 youths in GBV fight

Romeo Umali

Veep attends inauguration of new St. Patrick’s Church

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.