Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Mphenzi yapha asodzi awiri ku Mangochi

Asodzi awiri afa panyanja ya Malawi mphenzi itawaomba, malinga ndi ofalitsa nkhani pa polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daudi.

A Daudi ati ngoziyi yachitika mdera la mfumu Moto mdera la mfumu yaikulu Namabvi.

“Tamvetsedwa kuti asodziwa anali panyanja kugwira ntchito yawo monga mwamasiku onse koma mwadzidzi kunayamba mphepo ya mwera ndi mvula yamphamvu yophatikizana ndi mphenzi yomwe inaomba bwato lawo,” a Daudi anatero.

Iwo anatinso chifukwa cha mphamvu za nyetsi ya mphenziyo, asodziwo anagwera m’madzi ndipo matupi awo apezeka atatentheka kwambiri.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Tisiya kutaya mkaka, alimi atero

Jeffrey Chinawa

Malawian Artists set to shine at Jamaica’s Reggae Month

MBC Online

ALIMI A MTEDZA APINDULA

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.